Masalmo 146

Cifoko ca munthu, cikhulupiriko ca Mulungu

1 Haleluya;

Ulemekeze Yehova, moyo wanga,

2 Ndidzalemekeza Yehovam’moyo mwanga;

Ndidzayimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

3 Musamakhulupirira zinduna,

Kapena mwana wa munthu, amene mulibe cipulumutso mwa iye.

4 Mpweya wace ucoka, abwerera kumka ku nthaka yace;

Tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zace zitayika.

5 Wodala munthu amene akhala naye Mulungu wa Yakobo kuti amthandize,

Ciyembekezo cace ciri pa Yehova, Mulungu wace;

6 Amene analenga zakumwamba ndi dziko lapansi,

Nyanja ndi zonse ziri m’mwemo;

Ndiye wakusunga coonadi kosatha:

7 Ndiye wakucitira ciweruzo osautsika;

Ndiye wakupatsa anjala cakudya;

Yehova amasula akaidi;

8 Yehova apenyetsa osaona;

Yehova aongoletsa onse owerama;

Yehova akonda olungama;

9 Yehova asunga alendo;

Agwiriziza mwana wamasiye mkazi wamasiye;

Koma akhotetsa njira ya oipa.

10 Yehova adzacita ufumu kosatha,

Mulungu wako, Ziyoni, ku mibadwo mibadwo.

Haleluya.