Alemekeze dzina la Mulungu cifukwa ca zokoma amacitira anthu ace
1 Haleluya;
Pakuti kuyimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma;
Pakuti cikondwetsa ici, cilemekezo ciyenera.
2 Yehova amanga Yerusalemu;
Asokolotsa otayika a Israyeli.
3 Aciritsa osweka mtima,
Namanga mabala ao.
4 Awerenga nyenyezi momwe ziri;
Azicha maina zonsezi.
5 Ambuye wathu ndi wamkuru ndi wa mphamvu zambiri;
Nzeru yace njosatha.
6 Yehova agwiriziza ofatsa;
Atsitsira oipa pansi.
7 Yamikani Yehova ndi kuthira mang’ombe;
Myimbireni Mulungu wathu zamlemekeza pazeze:
8 Amene aphimba thambo ndi mitambo,
Amene akonzera mvula nthaka,
Amene aphukitsa msipu pamapiri.
9 Amene apatsa zoweta cakudya cao,
Ana a khungubwi alikulira.
10 Mphamvu ya kavalo siimkonda:
Sakondwera nayo miyendo ya munthu.
11 Yehova akondwera nao akumuopa Iye,
Iwo akuyembekeza cifundo cace.
12 Yerusalemu, lemekezani Yehova;
Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.
13 Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu:
Anadalitsa ana anu m’kati mwanu.
14 Ndiyeamene akhalitsamalireanu mumtendere;
Akukhutitsani ndi tirigu wakuca bwino.
15 Atumiza lamulo lace ku dziko lapansi;
Mau ace athamanga liwiro.
16 Apatsa cipale cofewa ngati ubweya;
Awaza cisanu ngati phulusa.
17 Aponya matalala ace ngati zidutsu:
Adzaima ndani pa kuzizira kwace?
18 Atumiza mau ace nazisungunula;
Aombetsa mphepo yace, ayenda madzi ace.
19 Aonetsa mau ace kwa Yakobo;
Malemba ace, ndi maweruzo ace kwa Israyeli.
20 Sanatero nao anthu amtundu wina;
Ndipo za maweruzo ace, sanawadziwa.
Haleluya.