Miyambi 1

Zocitira miyambi

1 MIYAMBI ya Solomo mwana wa Davide, mfumu ya Israyeli.

2 Kudziwa nzeru ndi mwambo;

Kuzindikira mau ozindikiritsa;

3 Kulandira mwambo wakusamalira macitidwe,

Cilungamo, ciweruzo ndi zolunjika;

4 Kucenjeza acibwana,

Kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;

5 Kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira;

Ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

6 Kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lace,

Mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.

Munthu asalole oipa amcete

7 Kuopa Yehova ndiko ciyambi ca kudziwa;

Opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

8 Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,

Ndi kusasiya cilangizo ca amako

9 Pakuti izi ndi korona wa cisomo pamtu pako,

Ndi mkanda pakhosi pako.

10 Mwananga, akakukopa ocimwa usalole.

11 Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,

Tilalire osacimwa opanda cifukwa;

12 Tiwameze ali ndi moyo ngati manda,

Ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13 Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,

Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

14 Udzacita nafe maere,

Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;

15 Mwananga, usayende nao m’njira;

Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16 Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,

Afulumira kukhetsa mwazi.

17 Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;

18 Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.

19 Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;

Cilanda moyo wa eni ace,

Ceniezo la Nzeru

20 Nzeru ipfuula panja;

Imveketsa mau ace pabwalo;

21 Iitana posonkhana anthu polowera pacipata;

M’mudzi inena mau ace;

22 Kodi mudzakonda zacibwana kufikira liti, acibwana inu?

Onyoza ndi kukonda kunyoza,

Opusa ndi kuda nzeru?

23 Tembenukani pamene ndikudzudzulani;

Taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,

Ndikudziwitsani mau anga.

24 Cifukwa ndaitana, ndipo munakana;

Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;

25 Koma munapeputsa uphungu wangawonse,

Ndi kukana kudzudzula kwanga.

26 Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu,

Ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27 Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,

Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu;

Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.

28 Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera;

Adzandifunatu, osandipeza ai;

29 Cifukwa anada nzeru,

Sanafuna kuopa Yehova;

30 Anakana uphungu wanga,

Nanyoza kudzudzula kwanga konse;

31 Momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao,

Nadzakhuta zolingalira zao.

32 Pakuti kubwerera m’mbuyo kwa acibwana kudzawapha;

Ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

33 Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka,

Nadzakhala phe osaopa zoipa,