Ceniezo lakuti afune Nzeru nalewe njira za oipa
1 Ananu, mverani mwambo wa atate,
Nimuchere makutu mukadziwe luntha;
2 Pakuti ndikuphunzitsani zabwino;
Musasiye cilangizo canga.
3 Pakuti ndinali mwana kwa atate wanga,
Wokondedwa ndi mai, ndine ndekha, sanabala wina.
4 Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine,
Mtima wako uumirire mau anga;
Sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.
5 Tenga nzeru, tenga luntha;
Usaiwale, usapatuke pa mau a m’kamwa mwanga;
6 Usasiye nzeru, ndipo Idzakusunga;
Uikonde, idzakucinjiriza.
7 Nzeru ipambana, tatenga nzeru;
M’kutenga kwako konseko utenge luntha.
8 Uilemekeze, ndipo idzakukweza;
Idzakutengera ulemu pamene uifungatira.
9 Idzaika cisada ca cisomo pamtu pako;
Idzakupatsa korona wokongola.
10 Tamvera mwananga, nulandire mau anga;
Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.
11 Ndakuphunzitsa m’njira ya nzeru,
Ndakuyendetsa m’mayendedwe olungama.
12 Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;
Ukathamanga, sudzapunthwa.
13 Gwira mwambo, osauleka;
Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.
14 Usalowe m’mayendedwe ocimwa,
Usayende m’njira ya oipa.
15 Pewapo, osapitamo;
Patukapo, nupitirire.
16 Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona;
Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.
17 Pakuti amadya cakudya ca ucimo,
Namwa vinyo wa cifwamba.
18 Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbanda kuca,
Kunkabe kuwala kufikira usana woti mbe.
19 Njira ya oipa ikunga mdima;
Sadziwa cimene ciwapunthwitsa,
20 Mwananga, tamvera mau anga;
Cherera makutu ku zonena zanga.
21 Asacoke ku maso ako;
Uwasunge m’kati mwa mtima wako.
22 Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza,
Nalamitsa thupi lao lonse.
23 Cinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga;
Pakuti magwero a moyo aturukamo.
24 Tasiya m’kamwa mokhota,
Uike patari milomo yopotoka.
25 Maso ako ayang’ane m’tsogolo,
Zikope zako zipenye moongoka,
26 Sinkasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako;
Njira zako zonse zikonzeke.
27 Usapatuke ku dzanja lamanja kapena kulamanzere;
Suntha phazi lako kusiya zoipa.