Miyambi 10

Miyambo yosiyana-siyana; Miyambo ya Sotomo

1 Mwana wanzeru akondweretsa atate;

Koma mwana wopusa amvetsa amace cisoni.

2 Cuma ca ucimo sicithangata:

Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

3 Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;

Koma amainga cifuniro ca wocimwa.

4 Wocita ndi dzanja laulesi amasauka;

Koma dzanja la akhama lilemeretsa.

5 Wokolola m’malimwe ndi mwana wanzeru;

Koma wogona pakututa ndi mwana wocititsa manyazi.

6 Madalitso ali pamtu pa wolungama

Koma m’kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

7 Amayesa wolungama wodala pamkumbukira;

Koma dzina la oipa lidzabvunda.

8 Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;

Koma citsiru colongolola cidzagwa.

9 Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;

Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.

10 Wotsinzinira acititsa cisoni;

Koma wodzudzula momveka acita mtendere.

11 M’kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;

Koma m’kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

12 Udani upikisanitsa;

Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.

13 Nzeru ipezedwa m’milomo ya wozindikira;

Koma wopusa pamsana pace ntyole.

14 Anzeru akundika zomwe adziwa

Koma m’kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.

15 Cuma ca wolemera ndi mudzi wace wolimba;

Koma umphawi wao uononga osauka.

16 Nchito za wolungama zipatsa moyo;

Koma phindu la oipa licimwitsa.

17 Wosunga mwambo ali m’njira ya moyo;

Koma wosiya cidzudzulo asocera.

18 Wobisa udani ali ndi milomo yonama;

Wonena ugogodi ndiye citsiru.

19 Pocuruka mau zolakwa sizisoweka;

Koma wokhala cete acita mwanzeru.

20 Lilime la wolungama likunga siliva wosankhika;

Koma mtima wa oipa uli wacabe.

21 Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri;

Koma zitsiru zimafa posowa nzeru.

22 Madalitso a Yehova alemeretsa,

Saonjezerapo cisoni.

23 Masewero a citsiru ndiwo kucita zoipa;

Koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

24 Comwe woipa aciopa cidzamfikira;

Koma comwe olungama acifuna cidzapatsidwa.

25 Monga kabvumvulu angopita, momwemo woipa kuti zi;

Koma olungama ndiwo maziko osatha.

26 Ngati vinyo wowawa m’mano, ndi utsi m’maso,

Momwemo wolesi kwa iwo amene amtuma.

27 Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku;

Koma zaka za oipa zidzafinimpha,

28 Ciyembekezo ca olungama ndico cimwemwe;

Koma cidikiro ca oipa cidzaonongeka.

29 Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;

Koma akucita zoipa adzaonongeka.

30 Wolungama sadzacotsedwa konse:

Koma oipa sadzakhalabe m’dziko.

31 M’kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru;

Koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32 Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa;

Koma m’kamwa mwa oipa munena zokhota,