1 Ndine duwa lofiira la ku Saroni,
Ngakhale kakombo wa kuzigwa.
2 Ngati kakombo pakati pa minga
Momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana akazi.
3 Ngati maula pakati pa mitengo ya m’nkhalango,
Momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana amuna.
Ndinakondwa pakukhala pa mthunzi wace,
Zipatso zace zinatsekemera m’kamwa mwanga.
4 Anandifikitsa ku nyumba ya vinyo,
Mbendera yace yondizolimira inali cikondi.
5 Mundilimbikitse ndi mphesa zouma, munditonthoze mtima ndi maula,
Pakuti ndadwala ndi cikondi.
6 Dzanja lace lamanzere anditsamiritse kumutu,
Dzanja lace lamanja ndi kundifungatira.
7 Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,
Pali mphoyo, ndi nswala za kuthengo,
Kuti musautse, ngakhale kugalamutsa cikondi,
Mpaka cikafuna mwini.
8 Mau a wokondedwa wanga mnyamatayo! Taona, adza,
Alikulumpha pamapiri, alikujidimuka pazitunda.
9 Wokondedwa wanga akunga mphoyo, pena mwana wa mbawala:
Taona, aima patseri pa khoma pathu,
Apenyera pazenera, Nasuzumira pamade.
10 Wokondedwa wanga analankhula, nati kwa ine,
Tauka, bwenzi langa, wokongola wanga, tiye.
11 Pakuti, taona, cisanu catha,
Mvula yapita yaleka;
12 Maluwa aoneka pansi;
Nthawi yoyimba mbalame yafika,
Mau a njiwa namveka m’dziko lathu;
13 Mkuyu uchetsa nkhuyu zace zosakhwima,
Mipesa niphuka,
Inunkhira bwino.
Tauka, bwenzi langa, wokongola wangawe, tiyetu.
14 Nkhunda yangawe, yokhala m’ming’alu ya thanthwe, mobisika motsetsereka,
Ndipenye nkhope yako, ndimve manako;
Pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.
15 Mutigwirire ankhandwe, ngakhale ang’ono, amene akuononga minda yamipesa;
Pakuti m’minda yathu yamipesa muphuka biriwiri.
16 Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wace:
Aweta zace pakati pa akakombo,
17 Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,
Bwera, bwenzi langawe, nukhale ngati mphoyo pena mwana wa mbawala
Pa mapiri a mipata.