Nyimbo 3

Mkwatibwi apeza mkwati

1 Usiku pamphasa panga ndinamfunafuna amene moyo wanga umkonda:

Ndinamfunafuna, koma osampeza.

2 Ndinati, Ndiuketu, ndiyendeyende m’mudzi,

M’makwalala ndi m’mabwalo ace,

Ndimfunefune amene moyo wanga umkonda:

Ndimfunafuna, koma osampeza.

3 Alonda akuyendayenda m’mudzi anandipeza:

Ndinati, Kodi munamuona amene moyo wanga umkonda?

4 Nditawapitirira pang’ono,

Ndinampeza amene moyo wanca umkonda:

Ndinamgwiriziza, osamfumbatula,

Mpaka nditamlowetsa m’nyumba ya amai,

Ngakhale m’cipinda ca wondibala.

5 Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,

Pali mphoyo, ndi nswala ya kuthengo,

Kuti musautse, ngakhale kugalamutsa cikondi,

Mpaka cikafuna mwini.

Ulendo wa ukwati

6 Ndaniyu akwera kuturuka m’cipululu ngati utsi wa tolo,

Wonunkhira ndi nipa ndi mtanthanyerere,

Ndi zonunkhiritsa zonse za wogulitsa?

7 Taonani, ndi macila a Solomo;

Pazingapo amuna amphamvu makumi asanu ndi limodzi,

A mwa ngwazi za Israyeli.

8 Onsewo agwira lupanga, nazolowera nkhondo:

Yense ali ndi lupanga lace pancafu pace,

Cifukwa ca upandu wa usiku.

9 Solomo mfumu anadzipangira macila okhalamo tsonga

Ndi matabwa a ku Lebano.

10 Anapanga timilongoti tace ndi siliva,

Ca pansi pace ndi golidi, mpando wace ndi nsaru yakuda,

Pakati pace panayalidwa za cikondi ca ana akazi a ku Yerusalemu.

11 Turukani, ana akazi inu a Ziyoni, mupenye Solomo mfumu,

Ndi korona amace anambveka naye tsiku la ukwati wace,

Ngakhale tsiku lakukondwera mtima wace.