Nyimbo 8

1 Mwenzi utakhala ngati mlongwanga,

Woyamwa pa bere la amai!

Ndikadakupeza panja, ndikadakupsompsona;

Osandinyoza munthu.

2 Ndikadakutsogolera, kukulowetsa m’nyumba ya amai,

Kuti andilange mwambo; Ndikadakumwetsa vinyo wokoleretsa,

Ndi madzi a makangaza anga.

3 Dzanja lamanzere lace akadanditsamiritsa kumutu,

Lamanja lace ndi kundifungatira.

4 Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,

Muutsiranji, mugalamutsiranji cikondi,

Cisanafune mwini.

5 Ndaniyu acokera kucipululu,

Alikutsamira bwenzi lace?

Pa tsinde la muula ndinakugalamutsa mnyamatawe:

Pomwepo amako anali mkusauka nawe,

Pomwepo wakukubala anali m’pakati pa iwe.

6 Undilembe pamtima pako, mokhoma cizindikilo, nundikhomenso cizindikilo pamkono pako;

Pakuti cikondi cilimba ngati imfa;

Njiru imangouma ngati manda:

Kung’anima kwace ndi kung’anima kwa moto,

Ngati mphezi ya Yehova,

7 Madzi ambiri sangazimitse cikondi,

Ngakhale mitsinje yodzala kucikokolola:

Mwamuna akapereka katundu yense wa m’nyumba yace ngati sintho la cikondi,

Akanyozedwa ndithu.

8 Tiri ndi mlongwathu wamng’ono,

Alibe maere;

Ticitirenji mlongwathu

Tsiku lokhoma unkhoswe wace?

9 Ngati ndiye khoma, tidzamanga pa iye nsanja yasiliva:

Ngati ndiye citseko tidzamtsekereza ndi matabwa amikungudza.

10 Ndine khoma, maere anga akunga nsanja zace:

Pamaso pa mnyamatayo ndinafanana ngati wopeza mtendere.

11 Solomo anali ndi munda wamipesa ku Baalahamoni;

Nabwereka alimi mundawo;

Yense ambwezere ndalama cikwi cifukwa ca zipatso zace.

12 Koma munda wanga wamipesa, uli pamaso panga ndiwo wangatu;

Naco cikwico, Solomo iwe,

Koma olima zipatso zace azilandira mazana awiri.

13 Namwaliwe wokhala m’minda,

Anzake amvera mau ako:

Nanenso undimvetse.

14 Dzifulumira, mnyamatawe wokondedwa wanga,

Dzifanane ngati mphoyo pena mwana wa mbawala

Pa mapiri a mphoka,