Yona 2

Pemphero la Yona ali m’mimba mwa cinsomba

1 Pamenepo Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wace ali m’mimba mwa nsombayo.

2 Ndipo anati,

Ndinaitana Yehova m’nsautso yanga,

Ndipo anandiyankha ine;

Ndinapfuula ndiri m’mimba ya manda,

Ndipo munamva mau anga.

3 Pakuti munandiponya mwakuya m’kati mwa nyanja,

Ndipo madzi anandizinga;

Mapfunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.

4 Ndipo ndinati, Ndatayika ndicoke pamaso panu;

Koma ndidzapenyanso Kacisi wanu wopatulika.

5 Madzi anandizinga mpaka moyo wanga,

Madzi akuya anandizungulira,

Kayandeyande wa m’nyanja anandikulunga mutu.

6 Ndinatsikira ku matsinde a mapiri,

Mipingiridzo ya dziko inanditsekereza kosatha;

Koma munandikwezera moyo wanga kuucotsa kucionongeko, Yehova Mulungu wanga.

7 Pokomoka moyo wanga m’kati mwanga ndinakumbukila Yehova;

Ndi pemphero langa linafikira Inu m’Kacisi wanu wopatulika.

8 Iwo osamalira mabodza opanda pace

Ataya cifundo cao cao.

9 Koma ine ndidzakupherani Inu nsembe ndi mau akuyamika,

Ndidzakwaniritsacowindacanga.

Cipulumutso nca Yehova.

10 Pamenepo Yehova analankhula ndi nsombayo, ndipo inamsanzira Yona kumtunda.