Yobu 25

Bilidadi akuti munthu sayenera kudziyesa wolungama pamaso pa Mulungu

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha, nati,

2 Kulamulira ndi kuopsa kuti ndi Iye;

Acita mtendere pa zam’mwamba zace.

3 Ngati awerengedwa makamu ace?

Ndipo ndaniyo, kuunika kwace sikumturukira?

4 Potero munthu akhala bwanji wolungama kwa Mulungu?

Kapena wobadwa ndi mkazi akhala woyera bwanji?

5 Taonani, ngakhale mwezi ulibe kuwala;

Ndi nyenyezi siziyera pamaso pace;

6 Kopambana kotani nanga munthu, ndiye mphutsi!

Ndi wobadwa ndi munthu, ndiyo nyongolotsi!