Nyimbo 7

1 Ha, mapazi ako akongola m’zikwakwata,

Mwana wamkaziwe wa mfumu!

Pozinga m’cuuno mwako pakunga zonyezimira,

Nchito ya manja a mmisiri waluso.

2 Pamcombo pako pakunga cikho coulungika,

Cosasowamo vinyo wosanganika:

Pamimba pako pakunga mulu wa tirigu

Wozingidwa ndi akakombo.

3 Maere ako akunga ana awiri a nswala

Anabadwa limodzi.

4 Khosi lako likunga nsanja yaminyanga;

Maso ako akunga matawale a ku Hesiboni,

A pa cipata ca Batirabimu;

Mphuno yako ikunga nsanja ya ku Lebano

Imene iloza ku Damasiko.

5 Mutu wako ukunga Karimeli,

Ndi tsitsi la pamtu pako likunga nsaru yakuda;

Mfumu yamangidwa ndi nkhata zace ngati wamsinga.

6 Ha, ndiwe wokongola ndi wofunika,

Bwenziwe, m’zokondweretsa!

7 Msinkhu wakowu ukunga mlaza,

Maere ako akunga matsango amphesa,

8 Ndinati, Ndikakwera pamlazapo,

Ndikagwira nthambi zace:

Maere ako ange ngati matsango amphesa,

Ndi kununkhira kwa mpweya wako ngati maula;

9 M’kamwa mwako munge ngati vinyo woposa,

Womeza tseketeke bwenzi langa,

Wolankhulitsa milomo ya ogona tulo.

10 Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo,

Ndine amene andifunayo.

11 Tiye, bwenzi langa, tinke kuminda;

Titsotse m’miraga.

12 Tilawire kunka ku minda yamipesa;

Tiyang’ane ngati mpesa waphuka, kunje ndi kuonetsa zipatso,

Makangaza ndi kutuwa maluwa ace;

Pompo ndidzakupatsa cikondi canga,

13 Mandimu anunkhira,

Ndi pamakomo pathu zipatso zabwino, za mitundu mitundu, zakale ndi zatsopano,

Zimene ndakukundikira iwe, wokondedwa wanga.