Miyambi 3

Malangizo a kuopa, kukhulupira, ndi kumvera Yehova

1 Mwananga, usaiwale malamulo anga,

Mtima wako usunge malangizo anga;

2 Pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,

Ndi zaka za moyo ndi mtendere.

3 Cifundo ndi coonadi zisakusiye;

Uzimange pakhosi pako;

Uzilembe pamtima pako;

4 Motero udzapezakisomo ndi nzeru yabwino,

Pamaso pa Mulungu ndi anthu.

5 Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,

Osacirikizika pa luntha lako;

6 Umlemekeze m’njira zako zonse,

Ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

7 Usadziyese wekha wanzeru;

Opa Yehova, nupatuke pazoipa;

8 Mitsempha yako idzalandirapo moyo,

Ndi mafupa ako uwisi.

9 Lemekeza Yehova ndi cuma cako,

Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;

10 Motero nkhokwe zako zidzangoti the,

Mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11 Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,

Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;

12 Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;

Monga atate mwana amene akondwera naye.

Phindu la Nzeru

13 Wodala ndi wopeza nzeru,

Ndi woona luntha;

14 Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,

Phindu lace liposa golidi woyengeka.

15 Mtengo wace uposa ngale;

Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

16 Masiku ambiri ali m’dzanja lamanja lace;

Cuma ndi ulemu m’dzanja lace lamanzere.

17 Njira zace ziri zokondweretsa,

Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.

18 Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;

Wakulumirira ngwodala.

19 Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;

Naika zamwamba ndi luntha.

20 Zakuya zinang’ambika ndi kudziwakwace;

Thambo ligwetsa mame.

21 Mwananga, zisacokere ku maso ako;

Sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

22 Ndipo mtima wako udzatengapo moyo,

Ndi khosi lako cisomo.

23 Pompo udzayenda m’njira yako osaopa,

Osapunthwa phazi lako.

24 Ukagona, sudzacita mantha;

Udzagona tulo tokondweretsa.

25 Usaope zoopsya zodzidzimutsa,

Ngakhale zikadza zopasula oipa;

26 Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,

Nadzasunga phazi lako lingakodwe.

Malangizo ena osiyana

27 Oyenera kulandira zabwino usawamane;

Pokhoza dzanja lako kuwacitira zabwino.

28 Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,

Ndipo mawa ndidzakupatsa;

Pokhala uli nako kanthu.

29 Usapangire mnzako ciwembu;

Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.

30 Usakangane ndi munthu cabe,

Ngati sanakucitira coipa,

31 Usacitire nsanje munthu waciwawa;

Usasankhe njira yace iri yonse.

32 Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;

Koma cinsinsi cace ciri ndi oongoka.

33 Mulungu atemberera za m’nyumba ya woipa;

Koma adalitsa mokhalamo olungama.

34 Anyozadi akunyoza,

Koma apatsa akufatsa cisomo.

35 Anzeru adzalandira ulemu colowa cao;

Koma opusa adzakweza manyazi.