Miyambi 2

Ukoma ndi phindu tace la Nzeru

1 Mwananga, ukalandira mau anga,

Ndi kusunga malamulo anga;

2 Kucherera makutu ako kunzeru,

Kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

3 Ukaitananso luntha,

Ndi kupfuulira kuti ukazindikire;

4 Ukaifunafuna ngati siliva,

Ndi kuipwaira ngati cuma cobisika;

5 Pompo udzazindikira kuopa Yehova

Ndi kumdziwadi Mulungu.

6 Pakuti Yehova apatsa nzeru;

Kudziwa ndi kuzindikira kuturuka m’kamwa mwace;

7 Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni;

Ndiye cikopa ca oyenda molunjika;

8 Kuti acinjirize njira za ciweruzo,

Nadikire khwalala la opatulidwa ace.

9 Pamenepo udzazindikira cilungamo ndi ciweruzo,

Zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10 Pakuti nzeru idzalowa m’mtima mwako,

Moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

11 Kulingalira kudzakudikira,

Kuzindikira kudzakucinjiriza;

12 Kukupulumutsa ku njira yoipa,

Kwa anthu onena zokhota;

13 Akusiya mayendedwe olungama,

Akayende m’njira za mdima;

14 Omwe asangalala pocita zoipa,

Nakondwera ndi zokhota zoipa;

15 Amene apotoza njira zao,

Nakhotetsa mayendedwe ao;

16 Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi waciwerewere,

Kwa mkazi wacilendo wosyasyalika ndi mau ace;

17 Wosiya bwenzi la ubwana wace,

Naiwala cipangano ca Mulungu wace;

18 Nyumba yace itsikira kuimfa,

Ndi mayendedwe ace kwa akufa;

19 Onse akunka kwa iye sabweranso,

Safika ku njira za moyo;

20 Nzeru idzakuyendetsa m’njira ya anthu abwino,

Kuti usunge mayendedwe a olungama.

21 Pakuti oongoka mtima adzakhala m’dziko,

Angwiro nadzatsalamo.

22 Koma oipa adzalikhidwa m’dziko,

Aciwembu adzazulidwamo.