Miyambi 18

1 Wopanduka afunafuna niro cace,

Nakangana ndi nzeru yonse yeniyeni.

2 Wopusa sakondwera ndi kuzindikira;

Koma kungobvumbulutsa za m’mtima mwace.

3 Pakudza wamphulupulu padzanso kunyoza;

Manyazi natsagana ndi citonzo.

4 Mau a m’kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya;

Kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.

5 Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankhu sikuli kwabwino,

Ngakhale kucitira cetera wolungama.

6 Milomo ya wopusa ifikitsa makangano;

Ndipo m’kamwa mwace muputa kukwapulidwa.

7 M’kamwa mwa wopusa mumuononga,

Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.

8 Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,

Zotsikira m’kati mwa mimba.

9 Wogwira nchito mwaulesi

Ndiye mbale wace wa wosakaza.

10 Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;

Wolungama athamangiramo napulumuka.

11 Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;

Alingalira kuti ndico khoma lalitari.

12 Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;

Koma cifatso citsogolera ulemu.

13 Wobwezera mau asanamvetse apusa,

Nadzicititsa manyazi.

14 Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;

Koma ndani angatukule mtima wosweka?

15 Mtima wa wozindikira umaphunzira;

Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

16 Mtulo wa munthu umtsegulira njira,

Numfikitsa pamaso pa akuru.

17 Woyamba kudzinenera ayang’anika wolungama;

Koma mnzace afika namuululitsa zace zonse.

18 Ula uletsa makangano,

Nulekanitsa amphamvu.

19 Kupembedza mbale utamcimwira nkobvuta,

Kulanda mudzi wolimba nkosabvuta;

Makangano akunga mipiringidzo ya linga.

20 Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m’kamwa mwace;

Iye nadzakhuta phindu la milomo yace.

21 Lilime liri ndi mphamvu pa imfa ndi moyo;

Wolikonda adzadya zipatso zace.

22 Wopeza mkazi apeza cinthu cabwino;

Yehova amkomera mtima.

23 Wosauka amadandaulira;

Koma wolemera ayankha mwaukali.

24 Woyanjana ndi ambiri angodziononga;

Koma liripo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.