Miyambi 14

1 Mkazi yense wanzeru amanga banja lace;

Koma wopusa alipasula ndi manja ace.

2 Woyenda moongoka mtima aopa Yehova;

Koma wokhota m’njira yace amnyoza,

3 M’kamwa mwa citsiru muli ntyole ya kudzikuza;

Koma milomo ya anzeru Idzawasunga.

4 Popanda zoweta modyera muti see;

Koma mphamvu ya ng’ombe icurukitsa phindu.

5 Mboni yokhulupirika sidzanama;

Koma mboni yonyenga imalankhula zonama.

6 Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;

Koma wozindikira saona bvuto m’kuphunzira.

7 Pita pamaso pa munthu wopusa,

Sudzazindikira milomo yakudziwa.

8 Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace;

Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.

9 Zitsiru zinyoza kuparamula;

Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.

10 Mtima udziwa kuwawa kwace kwace;

Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.

11 Nyumba ya oipa idzapasuka;

Koma hema wa oongoka mtima adzakula.

12 Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;

Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

13 Ngakhale m’kuseka mtima uwawa;

Ndipo matsiriziro a ciphwete ndi cisoni.

14 Wobwerera m’mbuyo m’mtima adzakhuta njira zace;

Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.

15 Wacibwana akhulupirira mau onse;

Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.

16 Wanzeru amaopa nasiya zoipa;

Koma wopusa amanyada osatekeseka.

17 Wokangaza kukwiya adzacita utsiru;

Ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.

18 Acibwana amalandira colowa ca utsiru;

Koma ocenjera amabvala nzeru ngati korona.

19 Oipa amagwadira abwino,

Ndi ocimwa pa makomo a olungama.

20 Waumphawi adedwa ndi anzace omwe;

Koma akukonda wolemera acuruka.

21 Wonyoza anzace acimwa;

Koma wocitira osauka cifundo adala.

22 Kodi oganizira zoipa sasocera?

Koma akuganizira zabwino adzalandira cifundo ndi ntheradi.

23 M’nchito zonse muli phindu;

Koma kulankhula-lankhula kungopatsa umphawi.

24 Korona wa anzeru ndi cuma cao;

Utsiru wa opusa ndiwo utsiru.

25 Mboni yoona imalanditsa miyoyo;

Koma wolankhula zonama angonyenga.

26 Wakuopa Yehova akhulupirira kolimba;

Ndipo ana ace adzakhala ndi pothawirapo.

27 Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo,

Kupatutsa ku misampha ya imfa.

28 Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu;

Koma popanda anthu kalonga aonongeka.

29 Wosakwiya msanga apambana kumvetsa;

Koma wansontho akuza utsiru.

30 Mtima wabwino ndi moyo wa thupi;

Koma nsanje ibvunditsa mafupa.

31 Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wace;

Koma wocitira wosauka cifundo amlemekeza.

32 Wocimwa adzakankhidwa m’kuipa kwace;

Koma wolungama akhulupirirabe pomwalira,

33 Nzeru ikhalabe m’mtima wa wozindikira,

Nidziwika pakati pa opusa.

34 Cilungamo cikuza mtundu wa anthu;

Koma cimo licititsa pfuko manyazi.

35 Mfumu ikomera mtima kapolo wocita mwanzeru;

Koma idzakwiyira wocititsa manyazi.