Miyambi 13

1 Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate;

Koma wonyoza samvera cidzudzulo.

2 Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m’kamwa mwace;

Koma moyo wa aciwembu udzadya ciwawa.

3 Wogwira pakamwa pace asunga moyo wace;

Koma woyasamula milomo yace adzaonongeka.

4 Moyo wa wolesi ukhumba osalandira kanthu;

Koma moyo wa akhama udzalemera.

5 Wolungama ada mau onama;

Koma woipa anyansa, nadzicititsa manyazi,

6 Cilungamo cicinjiriza woongoka m’njira;

Koma udio ugwetsa wocimwa.

7 Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;

Alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi cuma cambiri.

8 Ciombolo ca moyo wa munthu ndico cuma cace;

Koma wosauka samva cidzudzulo.

9 Kuunika kwa olungama kukondwa;

Koma nyali ya oipa idzazima.

10 Kudzikuza kupikisanitsa;

Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

11 Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;

Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.

12 Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima;

Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.

13 Wonyoza mau adziononga yekha;

Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14 Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,

Apatutsa ku misampha ya imfa.

15 Nzeru yabwino ipatsa cisomo;

Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.

16 Yense wocenjera amacita mwanzeru:

Koma wopusa aonetsa utsiru.

17 Mthenga wolakwa umagwa m’zoipa;

Koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.

18 Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;

Koma wolabadira cidzudzulo adzalemekezedwa.

19 Cifuniro cikondweretsa moyo citacitidwa;

Koma kusiya zoipa kunyansa opusa,

20 Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:

Koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

21 Zoipa zilondola ocimwa;

Koma olungama adzalandira mphotho yabwino.

22 Wabwino asiyira zidzukulu zace colowa cabwino;

Koma wocimwa angosungira wolungama cuma cace.

23 M’kulima kwa osauka muli zakudya zambiri;

Koma zinazo zimaonongeka posowa ciweruzo.

24 Wolekereramwanace osammenya amuda;

Koma womkonda amyambize kumlanga.

25 Wolungama adya nakhutitsa moyo wace;

Koma mimba ya oipa idzasowa.