Miyambi 12

1 Wokonda mwambo akonda kudziwa;

Koma wakuda cidzudzulo apulukira.

2 Yehova akomera mtima munthu wabwino;

Koma munthu wa ziwembu amtsutsa,

3 Munthu sadzakhazikika ndi udio,

Muzu wa olungama sudzasunthidwa.

4 Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace;

Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.

5 Maganizo a olungama ndi ciweruzo;

Koma uphungu wa oipa unyenga.

6 Mau a oipa abisalira mwazi;

Koma m’kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7 Oipa amagwa kuli zi;

Koma banja la olungama limaimabe.

8 Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;

Koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9 Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,

Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10 Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;

Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.

11 Zakudyazikwanira wolima minda yace;

Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.

12 Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;

Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13 M’kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;

Koma wolungama amaturuka m’mabvuto.

14 Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m’kamwa mwace;

Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.

15 Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;

Koma wanzeru amamvera uphungu.

16 Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;

Koma wanzeru amabisa manyazi.

17 Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;

Koma mboni yonama imanyenga.

18 Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;

Koma lilime la anzeru lilamitsa.

19 Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;

Koma lilime lonama likhala kamphindi.

20 Cinyengo ciri m’mitima ya oganizira zoipa;

Koma aphungu a mtendere amakondwa.

21 Palibe bvuto lidzagwera wolungama;

Koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa,

22 Milomo yonama inyansa Yehova;

Koma ocita ntheradi amsekeretsa.

23 Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;

Koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.

24 Dzanja la akhama lidzalamulira;

Koma wolesi adzakhala ngati kapolo,

25 Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu;

Koma mau abwino aukondweretsa.

26 Wolungama atsogolera mnzace;

Koma njira ya oipa iwasokeretsa.

27 Wolesi samaocha nyama yace anaigwira;

Koma wolungama amalandira cuma copambana ca anthu.

28 M’khwalala la cilungamo muli moyo;

M’njira ya mayendedwe ace mulibe imfa.