Miyambi 11

1 Muyeso wonyenga unyansa Yehova;

Koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

2 Pakudza kudzikuza padzanso manyazi;

Koma nzeru iri ndi odzicepetsa,

3 Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera;

Koma kukhota kwa aciwembu kudzawaononga.

4 Cuma sicithandiza tsiku la mkwiyo;

Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

5 Cilungamo ca wangwiro cimaongola njira yace;

Koma woipa adzagwa ndi zoipa zace.

6 Cilungamo ca oongoka mtima cidzawapulumutsa;

Koma aciwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

7 Pomwalira woipa cidikiro cace cionongeka;

Ciyembekezo ca ucimo cionongeka.

8 Wolungama apulumuka kubvuto;

Woipa nalowa m’malo mwace.

9 Wonyoza Mulungu aononga mnzace ndi m’kamwa mwace;

Koma olungama adzapulumuka pakudziwa,

10 Olungama akapeza bwino, mudzi usekera;

Nupfuula pakuonongeka oipa.

11 Madalitso a olungama akuza mudzi;

Koma m’kamwa mwa oipa muupasula.

12 Wopeputsa mnzace asowa nzeru;

Koma wozindikira amatonthola.

13 Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;

Koma wokhulupirika mtima abisa mau.

14 Popanda upo wanzeru anthu amagwa;

Koma pocuruka aphungu pali cipulumutso.

15 Woperekera mlendo cikole adzaphwetekwapo;

Koma wakuda cikole akhala ndi mtendere.

16 Mkazi wodekha agwiritsa ulemu;

Aukali nagwiritsa cuma.

17 Wacifundo acitira moyo wace zokoma;

Koma wankhanza abvuta nyama yace.

18 Woipa alandira malipiro onyenga;

Koma wofesa cilungamo aonadi mphotho,

19 Wolimbikira cilungamo alandira moyo;

Koma wolondola zoipa adzipha yekha,

20 Okhota mtima anyansa Yehova;

Koma angwiro m’njira zao amsekeretsa.

21 Zoonadi, wocimwa sadzapulumuka cilango;

Koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.

22 Monga cipini cagolidi m’mphuno ya nkhumba,

Momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.

23 Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha;

Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.

24 Alipo wogawira, nangolemerabe;

Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.

25 Mtima wa mataya udzalemera;

Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

26 Womana tirigu anthu amtemberera;

Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.

27 Wopwaira ubwino afunitsa cikondwerero;

Koma zoipa zidzamfikira wozilondola.

28 Wokhulupmra cuma cace adzagwa;

Koma olungama adzaphuka ngati tsamba.

29 Wobvuta banja lace adzalowa m’zomsautsa;

Wopusa adzatumikira wanzeru.

30 Cipatso ca wolungama ndi mtengo wa moyo;

Ndipo wokola mtima ali wanzeru.

31 Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno;

Koposa kotani woipa ndi wocimwa?