Masalmo 85

Akumbutsa Mulungu madalitso akale, apempha awabwereze

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Satmo la ana a Kora.

1 Munacita zobvomereza dziko lanu, Yehova;

Munabweza ukapolo wa Yakobo.

2 Munacotsa mphulupulu ya anthu anu,

Munafotsera zolakwa zao zonse.

3 Munabweza kuzaza kwanu konse;

Munabwerera ku mkwiyo wanu wotentha.

4 Mutibweze, Mulungu wa cipulumutso cathu,

Nimuletse udani wanu wa pa ife.

5 Kodi mudzatikwiyira nthawi zonse?

Kodi mudzakhala cikwiyire mibadwo mibadwo?

6 Kodi simudzatipatsanso moyo,

Kuti anthu anu akondwerere ndi Inu?

7 Tionetseni cifundo canu, Yehova,

Tipatseni cipulumutso canu.

8 Ndidzamva colankhula Mulungu Yehova;

Pakuti adzalankhula zamtendere ndi anthu ace, ndi okondedwa ace;

Koma asabwererenso kucita zapusa.

9 Indedi cipulumutso cace ciri pafupi ndi iwo akumuopa Iye;

Kuti m’dziko mwathu mukhale ulemu.

10 Cifundo ndi coonadi zakomanizana;

Cilungamo ndi mtendere zapsompsonana,

11 Coonadi ciphukira m’dziko;

Ndi cilungamo casuzumira ciri m’mwamba.

12 Inde Yehova adzapereka zokoma;

Ndipo dziko lathu lidzapereka zipatso zace.

13 Cilungamo cidzamtsogolera; Nicidzamkonzera mapazi ace njira.