Masalmo 84

Okhala m’nyumba ya Yehova ndiwo amwai

Kwa Mkulu wa Nyimbo, pa Gitili: Salmo la ana a Kora.

1 Pokhala Inu mpotikonda ndithu, Yehova wa makamu!

2 Moyo wanga ulakalaka, inde ukomokanso ndi kufuna mabwalo a Yehova;

Mtima wanga ndi thupi langa zipfuulira kwa Mulungu wamoyo.

3 Mbawanso inapeza nyumba,

Ndi namzeze cisa cace coikamo ana ace,

Pa maguwa a nsembe anu, Yehova wa makamu,

Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,

4 Odala iwo akugonera m’nyumba mwanu;

Akulemekezani cilemekezere,

5 Wodala munthu amene mphamvu yace iri mwa Inu;

Mumtima mwace muli makwalala a ku Ziyoni,

6 Popyola cigwa ca kulira misozi aciyesa ca akasupe;

Inde mvula: ya cizimalupsa icidzaza ndi madalitso.

7 Apita mwamphamvu naonjezapo mphamvu,

Aoneka pamaso pa Mulungu m’Ziyoni.

8 Yehova Mulungu wa makamu, imvani pemphero langa:

Cherani khutu, Mulungu wa Yakobo.

9 Onani, Mulungu, ndinu cikopa cathu;

Ndipo penyani pa nkhope ya Wodzozedwa wanu.

10 Pakuti tsiku limodzi m’mabwalo anu likoma koposa masiku ambirimbiri akukhala pena,

Kukhala inewapakhomo m’nyumba ya Mulungu wanga,

Kundikonda ine koposa kugonera m’mahema a coipa,

11 Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi cikopa;

Yehova adzapatsa cifundo ndi ulemerero;

Sadzakaniza cokoma iwo akuyenda angwiro,

12 Yehova wa makamu,

Wodala munthu wakukhulupirira Inu.