Masalmo 8

Davide ayimbira ulemerero wa Mulungu, ndi ulemu umene Mulungu acitira mtundu wa anthu

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Oititl. Salnto la Davide.

1 Yehova, Ambuye wathu,

Dzina lanu liposadi nanga pa dziko lonse lapansi!

Inu amene munaika ulemerero wanu pa thambo la kumwamba.

2 M’kamwa mwa makanda ndi oyamwamunakhazikitsamphamvu,

Cifukwa ca otsutsana ndi Inu,

Kuti muwaletse mdani ndi wobwezera cilango.

3 Pakuona ine thambo la kumwamba lanu, nchito ya zala zanu,

Mwezi ndi nyenyezi, zimene munazikhazika,

4 Munthu ndani kuti mumkumbukila?

Ndi mwana wa munthu kuti muceza naye?

5 Pakuti munamcepsa pang’ono ndi Mulungu,

Munambveka iye korona wa ulemerero ndi ulemu.

6 Munamcititsa ufumu pa nchito za manja anu;

Mudagonjetsa zonse pansi pa mapazi ace;

7 Nkhosa ndi ng’ombe, zonsezo,

Ndi nyama za kuthengo zomwe;

8 Mbalame za m’mlengalenga, ndi nsomba za m’nyanja.

Zopita m’njira za m’nyanja.

9 Yehova, Ambuye wathu,

Dzina lanu liposadi nanga pa dziko lonse lapansi!