Masalmo 75

Mulungu woweruza asiyanitsa pakati pa odzikuza ndi olungama

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Altasayeti: Salmo la Asafu. Nyimbo.

1 Tikuyamikani Inu, Mulungu; Tiyamika, pakuti dzina lanu liri pafupi;

Afotokozera zodabwiza zanu,

2 Pakuona nyengo yace ndidzaweruza molunjika.

3 Lasungunuka dziko lapansi, ndi onse okhalamo;

Ndinacirika mizati yace.

4 Ndinati kwa odzitamandira, Musamacita zodzitamandira;

Ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;

5 Musamakwezetsa nyanga yanu;

Musamalankhula ndi khosi louma.

6 Pakuti kukuzaku sikucokera kum’mawa,

Kapena kumadzulo, kapena kucipululu,

7 Pakuti Mulungu ndiye woweruza;

Acepsa wina, nakuza wina.

8 Pakuti m’dzanja la Yehova muli cikho;

Ndi vinyo wace acita thobvu;

Cidzala ndi zosanganizira, ndipo atsanulako:

Indedi, oipa onse a pa dziko lapansi adzamwa

Nadzagugudiza nsenga zace.

9 Koma ine ndidzalalikira kosalekeza,

Ndidzayimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.

10 Ndipo ndidzatseteka nyanga zonse za oipa;

Koma nyanga za wolungama zidzakwezeka.