Masalmo 61

Poopsedwa Davide athamangira Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo; Neginoto. Salmo la Davide.

1 Imvani mpfuu wanga, Mulungu;

Mverani pemphero langa.

2 Ku malekezero a dziko lapansi ndidzapfuulira kwa Inu, pomizika mtima wanga:

Nditsogolereni ku thanthwe londiposa ine m’kutalika kwace.

3 Pakuti munakhala pothawirapo panga; nsanja yolimba pathawa mdani ine.

4 Ndidzagonera-gonerabe m’cihemamwanu;

Ndidzathawira mobisalamo m’mapiko anu.

5 Pakuti Inu, Mulungu, mudamva zowinda zanga;

Munandipatsa colowa ca iwo akuopa dzina lanu.

6 Mudzatalikitsa moyo wa mfumu:

Zaka zace zidzafikira mibadwo mibadwo.

7 Adzakhala nthawi zonse pamaso pa Mulungu;

Mumpatse cifundo ndi coonadi zimsunge.

8 Potero ndidzayimba zolemekeza dzina lanu ku nthawi zonse,

Kuti ndicite zowinda zanga tsiku ndi tsiku.