Masalmo 60

Madandaulo ndi pempho la Davide

Kwa Mkulu wa Nyimbo pa Susan-Eduti. Miktamu wa Davide; lakulangiza: muja analimbana nao Aramnabaraimu ndi Aramzoba, nabwera Yoabu napha a Edomu m’Ciagwa ca Mcere zikwikhumi mpilambu Ziwiri.

1 Mwatitaya Mulungu, mwatipasula;

Mwakwiya; tibwezereni.

2 Mwagwedeza dziko, mwaling’amba:

Konzani ming’alu yace; pakuti ligwedezeka.

3 Mwaonetsa anthu anu zowawa:

Mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.

4 Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu,

Aikweze cifukwa ca coonadi.

5 Kuti okondedwa anu alanditsidwe,

Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja, ndipo mutibvomereze.

6 Mulungu walankhula m’ciyero cace; ndidzakondwerera:

Ndidzagawa Sekemu, ndidzayesa muyeso cigwa ca Sukoti.

7 Gileadi ndi wanga, Manasenso ndi wanga;

Ndipo Efraimu ndi mphamvu ya mutu wanga;

Yuda ndiye wolamulira wanga,

8 Moabu ndiye mkhate wanga;

Pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga:

Filistiya, pfuulatu cifukwa ca ine.

9 Adzandifikitsa ndani m’mudzi wa m’linga?

Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

10 Si ndinu, Mulungu, amene mwantaya?

Osaturuka nao makamu athu, Mulungu.

11 Tithandizeni kunsautso;

Kuti cipulumutso ca munthu ndi cabe.

12 Mwa Mulungu tidzacita molimbika mtima,

Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.