Masalmo 6

Davide apempha cifundo kwa Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto, pa Seminiti. Salmo la Davide.

1 Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,

Ndipo musandilange m’ukali wanu.

2 Mundicitire cifundo, Yehova; pakuti ndalefuka ine:

Mundicize, Yehova; pakuti anthunthumira mafupa anga.

3 Moyo wanganso wanthunthumira kwakukuru;

Ndipo Inu, Yehova, kufikira liti?

4 Bwererani Yehova, landitsani moyo wanga;

Ndipulumutseni cifukwa ca kukoma mtima kwanu.

5 Pakuti muimfa m’mosakumbukila Inu:

M’mandamo adzakuyamikani dani?

6 Ndalema nako kuusa moyo kwanga;

Ndiyandamitsa kama wanga usiku wonse;

Mphasa yanga ndiolobza ndi misozi yanga.

7 Lapuwala diso langa cifukwa ca cisoni;

Lakalamba cifukwa ca onse akundisautsa.

8 Cokani kwa ine, nonsenu akucita zopanda pace;

Pakuti wamva Yehova mau a kulira kwanaa,

9 Wamva Yehova kupemba kwanga;

Yehova adzalandira pemphero langa.

10 Adzacita manyazi, nadzanthunthumira kwakukuru adani anga onse;

Adzabwerera, nadzacita manyazi modzidzimuka,