Masalmo 58

Davide adzudzula oipa Mulungu awalange

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Altasyeti; Miktamu wa Davide.

1 Kodi muli cete ndithu poyenera inu kunena zolungama?

Muweruza ana a anthu molunjika kodi?

2 Inde, mumtima mucita zosalungama;

Pa dziko lapansi mugawira anthu ciwawa ca m’manja mwanu.

3 Oipa acita cilendo cibadwire:

Asokera kuyambira kubadwa kwao, nanena bodza.

4 Ululu wao ukunga wa njoka;

Akunga mphiri yogontha m’khutu, itseka m’khutu mwace.

5 Imene simvera liu la oitana,

Akucita matsenga mocenieratu,

6 Tyolani mano ao m’kamwa mwao, Mulungu:

Zulani zitsakano za misona ya mkango, Yehova.

7 Apitetu ngati madzi oyenda;

Popiringidza mibvi yace ikhale yodukaduka.

8 Apite ngati nkhono yosungunuka;

Asaone dzuwa monga mtayo,

9 Miphika yanu isanagwire moto waminga,

Adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.

10 Wolungama adzakondwera pakuona kubwezera cilango:

Adzasamba mapazi ace m’mwazi wa woipa.

11 Ndipo anthu adzati, Indedi, pali mphotho kwa wolungama;

Indedi, pali Mulungu wakuweruza pa dziko lapansi.