Masalmo 57

Davide apempha Mulungu amciniirize, namlemekezapo

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Altasheti Miktamu wa Davide: muja anathawa Sauli au m’phanga.

1 Mundicitire cifundo, Mulungu, mundicitire cifundo;

Pakuti moyo wanga ukhulupirira Inu:

Ndipo ndithawira ku mthunzi wa mapiko anu,

Kufikira zosakazazo zidzapita.

2 Ndidzapfuulira kwa Mulungu Wam’mwambamwamba;

Ndiye Mulungu wonditsirizira zonse.

3 Adzanditumizira m’mwamba, nadzandipulumutsa

Ponditonza wofuna kundimeza;

Mulungu adzatumiza cifundo cace ndi coonadi cace.

4 Moyo wanga uli pakati pa mikango;

Ndigona pakati pa oyaka moto,

Ndiwo ana a anthu amene mano ao ali nthungo ndi mibvi,

Ndipo lilime lao ndilio lupanga lakuthwa.

5 Mukwezeke m’mwambamwa mba, Mulungu;

Ulemerero wanu ukhale pamwamba pa dziko lonse lapansi.

6 Anandichera ukonde apo ndiyenda;

Moyo wanga wawerama:

Anandikumbira mbuna patsogolo panga;

Anagwa m’kati mwace iwo okha.

7 Mtima wanga wakhazikika, Mulungu, ndakhazika mtima;

Ndidzayimba, inde, ndidzayimba zolemekeza.

8 Galamuka, ulemu wanga; galamukani cisakasa ndi zeze:

Ndidzauka ndekha mamawa.

9 Ndidzakuyamikirani mwa anthu, Ambuye:

Ndidzakuyimbirani mwa mitundu.

10 Pakuti cifundo canu ncacikuru kufikira m’mwamba,

Ndi coonadi canu kufikira mitambo.

11 Kwezekani m’mwambamwamba, Mulungu;

Ulemerero wanu ukhale pamwamba m’dziko lonse lapansi.