Masalmo 56

Davide apempha Mulungu amlanditse; ayamika atamlanditsa

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Yonat-Elem Recokimu, Miktamu wa Davide, muja Afilisti anamgwira m’Gati.

1 Mundicitire cifundo, Mulungu, pakuti anthu afuna kundimeza:

Andipsinja pondithira nkhondo tsiku lonse.

2 Adani anga afuna kundimeza tsiku lonse:

Pakuti ambiri andithira nkhondo modzikuza.

3 Tsiku lakuopa ine,

Ndidzakhulupirira Inu.

4 Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ace:

Ndakhulupirira Mulungu, sindidzaopa;

Anthu adzandicitanji?

5 Tsiku lonse atenderuza mau anga:

Zolingirira zao zonse ziri pa ine kundicitira coipa.

6 Amemezana, alalira,

Achereza mapazi anga,

Popeza alindira moyo wanga.

7 Kodi adzapulumuka ndi zopanda pace?

Gwetsani anthu mumkwiyo, Mulungu.

8 Muwerenga kuthawathawa kwanga:

Sungani misozi yanga m’nsupa yanu;

Kodi siikhala m’buku mwanu?

9 Pamenepo adani anga adzabwerera m’mbuyo tsiku lakuitana ine:

Ici ndidziwa, kuti Mulungu abvomerezana nane.

10 Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ace:

Mwa Yehova ndidzalemekeza mau ace.

11 Pa Mulungu ndakhulupirira, sindidzaopa;

Munthu adzandicitanji?

12 Zowindira Inu Mulungu, ziri pa ine:

Ndidzakucitirani zoyamika.

13 Pakuti mwalanditsa moyo wanga kuimfa:

Simunatero nao mapazi anga kuti ndingagwe?

Kuti ndiyende pamaso pa Mulungu

M’kuunika kwa amoyo.