Masalmo 54

Davide apempha Mulungu amlanditse

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Cilangizo ca Davide. Muja Azift anamuka nauza Sauli, kuti, Kodi Davide sabisala kwathu nanga?

1 Ndipulumutseni, Mulungu, mwa dzina lanu,

Ndipo mundiweruze ndi mphamvuyanu.

2 Imvani pemphero langa, Mulungu;

Cherani khutu mau a pakamwa panga.

3 Pakuti alendo andiukira,

Ndipo oopsa afunafuna moyo wanga;

Sadziikira Mulungu pamaso pao.

4 Taonani, Mulungu ndiye mthandizi wanga:

Ambuye ndiye wacirikiza moyo wanga.

5 Adzabwezera coipa adani anga:

Aduleni m’coonadi canu.

6 Ine mwini ndidzapereka nsembe kwa Inu:

Ndidzayamika dzina lanu, Yehova, pakuti nlokoma.

7 Pakuti anandilanditsa m’nsautso yonse;

Ndipo ndapenya ndi diso langa ico ndakhumbira pa adani anga,