Kupusa ndi kuipa kwa anthu
Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Mahalat. Cilanidzo ca Davide.
1 Citsiru cimati mumtima mwace, Kulibe Mulungu.
Acita zobvunda, acita cosalungama conyansa;
Kulibe wakucita bwino.
2 Mulungu m’mwamba anaweramira pa ana a anthu,
Kuti aone ngati aliko wanzeru, Wakufuna Mulungu.
3 Onse anabwerera; anabvunda mtima pamodzi;
Palibe mmodzi wakucita bwino, nnena mmodzi.
4 Kodi ocita zopanda pace sadziwa?
Pomadya anthu anga monga akudya mkate;
Ndipo saitana Mulungu.
5 Pamenepo anaopa kwakukuru, popanda cifukwa ca kuopa:
Pakuti Mulungu anamwaza mafupa a iwo akuzinga iwe;
Unawacititsa manyazi, pakuti Mulungu anawakaniza.
6 Ha, cipulumutso ca Israyeli cicokere m’Ziyoni!
Pakubweretsa Mulungu anthu ace a m’ndende,
Yakobo adzakondwera, Israyeli adzasekera.