Masalmo 51

Davide abvomereza kucimwa kwace, apempha Mulungu amkhululukire, asamcotsere Mzimu Woyera

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davide; m’mene anamdzera Natani mnenertso atalowa iye kwa Bateseba.

1 Mundicitire ine cifundo, Mulungu,

Monga mwa kukoma mtima kwanu;

Monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu

Mufafanize macimo anga.

2 Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga,

Ndipo mundiyeretse kundicotsera coipa canga,

3 Cifukwa ndazindikira macimo anga;

Ndipo coipa canga ciri pamaso panga cikhalire:

4 Pa Inu, Inu nokha, ndinacimwa,

Ndipo ndinacicita coipaco pamaso panu:

Kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,

Mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.

5 Onani, ndinabadwa m’mphulupulu:

Ndipo mai wanga anandilandira m’zoipa.

6 Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m’malo a m’katimo;

Ndipo m’malo a m’tseri mudzandidziwitsa nzeru.

7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera;

Munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbu woposa matalala.

8 Mundimvetse cimwemwe ndi kusekera:

Kuti mafupawo munawatyola akondwere.

9 Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,

Ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.

10 Mundilengere mtima woyera, Mulungu;

Mukonze mzimu wokhazikika m’kati mwanga.

11 Musanditaye kundicotsa pamaso panu;

Musandicotsere Mzimu wanu Woyera.

12 Mundibwezere cimwemwe ca cipulumutso canu;

Ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

13 Pomwepo ndidzalangiza ocimwa njira zanu;

Ndipo olakwa adzabwera kwa Inu.

14 Mundilanditse ku mlandu wa mwazi, Mulungu,

Ndinu Mulungu wa cipulumutso canga;

Lilime langalidzakweza Nyimbo ya cilungamo canu.

15 Ambuye, tsegulani pa milomo yanga;

Ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.

16 Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka;

Nsembe yopsereza simuikonda.

17 Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka;

Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.

18 Citirani Ziyoni cokoma monga mwa kukondwera kwanu;

Mumange malinga a miyala a Yerusalemu.

19 Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zacilungamo,

Ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu:

Pamenepo adzapereka

Ng’ombe pa guwa lanu la nsembe.