Ukoma ndi ulemerero wa Ziyoni
Nyimbo; Salmo la ana a Kora.
1 Yehova ndiye wamkulu, ayenera kulemekezekadi,
M’mudzi wa Mulungu wathu, m’phiri lace loyera.
2 Phiri la Ziyoni, cikhalidwe cace ncokoma
Ku mbali zace za kumpoto,
Ndilo cimwemwe ca dziko lonse lapansi,
Mudzi wa mfumu yaikuru.
3 Mulungu adziwika m’zinyumba zace ngati msanje.
4 Pakuti, taonani, mafumuwo anasonkhana,
Anapitira pamodzi.
5 Anapenya mudziwo, ndipo pamenepo anadabwa;
Anaopsedwa, nathawako.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunthunthumira;
Anamva cowawa, ngati wam’cikuta.
7 Muswa zombo za ku Tarisi ndi mphepo ya kum’mawa.
8 Monga tidamva, momwemo tidapenya
M’mudzi wa Yehova wa makamu, m’mudzi wa Mulungu wathu:
Mulungu adzaukhazikitsa ku nthawi yamuyaya.
9 Tidalingalira za cifundo canu, Mulungu,
M’kati mwa Kacisi wanu.
10 Monga dzina lanu, Mulungu,
Momwemo lemekezo lanu ku malekezero a dziko lapansi:
M’dzanja lamanja lanu mudzala cilungamo.
11 Likondwere phiri la Ziyoni,
Asekere ana akazi a Yuda,
Cifukwa ca maweruzo anu.
12 Zungulirani Ziyoni, ndipo muuzinge;
Werengani nsanja zace.
13 Penyetsetsani malinga ace,
Yesetsani zinyumba zace;
Kuti mukaziwerengere mibadwo ikudza m’mbuyo.
14 Pakuti Mulungu ameneyo ndiye Mulungu wathu ku nthawi za nthawi:
Adzatitsogolera kufikira imfa.