Masalmo 47

Mau a kulemekeza Mulungu mwini dziko lonse lapansi

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la ana a Koro.

1 Ombani m’manja, mitundu yonse ya anthu;

Pfuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuyimbitsa.

2 Pakuti Yehova Wam’mwambamwamba ndiye woopsa;

Ndiye mfumu yaikuru pa dziko lonse lapansi.

3 Atigonjetsera anthu,

Naika amitundu pansi pa mapazi athu.

4 Atisankhira colowa cathu,

Cokometsetsa ca Yakobo amene anamkonda.

5 Mulungu wakwera ndi mpfuu,

Yehova ndi liu la lipenga.

6 Yimbirani Mulungu, yimbirani;

Yimbirani Mfumu yathu, yimbirani.

7 Pakuti Mulungu ndiye Mfumu ya dziko lonse lapansi;

Yimbirani ndi cilangizo.

8 Mulungu ndiye Mfumu ya amitundu:

Mulungu akhala pa mpando wacifumu wace woyera.

9 Akulu a anthu asonkhana

Akhale anthu a Mulungu wa Abrahamu:

Pakuti zikopa za dziko lapansi nza Mulungu;

Akwezeka kwakukuru Iyeyo.