Masalmo 42

Mtima wolira kuyanjana ndi Mulungu m’Kacisi

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Cilangizo ca kwa ana a Kora.

1 Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje;

Motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu.

2 Moyo wanga uli ndi ludzu la kwa Mulungu, la kwa Mulungu wamoyo:

Ndikadze liti kuoneka pamaso pa Mulungu?

3 Misozi yanga yakhalangati cakudya canga,

Usana ndi usiku;

Pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse,

Mulungu wako ali kuti?

4 Ndizikumbukila izi ndipo nditsanulira moyo wanga m’kati mwa ine,

Pakuti ndidafopita ndi unyinji wa anthu,

Ndinawatsogolera ku nyumba ya Mulungu, ndi mau akuyimbitsa ndi kuyamika,

Ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

5 Udziweramiranji moyo wanga iwe?

Ndi kuzingwa m’kati mwanga?

Yembekeza Mulungu, pakuti ndidzamyamikanso

Cifukwa ca cipulumutso ca nkhope yace.

6 Mulungu wanga, moyo wanga

Udziweramira m’kati mwanga;

Cifukwa cace ndikumbukila Inu m’dziko la Yordano,

Ndi mu Ahermone, m’kaphiri ka Mizara.

7 Madzi akuya aitanizana ndi madzi akuya,

Pa mkokomo wa matiti anu: Mafunde onse a nyondonyondo anandimiza ine.

8 Koma usana Yehova adzalamulira cifundo cace,

Ndipo usiku Nyimbo yace idzakhala ndi ine.

Inde pemphero la kwa Yehova wa moyowanga.

9 Ndidzati kwa Mulungu, thanthwe langa, mwandiiwala cifukwa ninji?

Ndimayenderanji wakulira Cifukwa ca kundipsinja mdaniyo?

10 Adani anga andinyoza ndi kundityola mafupa anga;

Pakunena ndine dzuwa lonse,

Mulungu wako ali kuti?

11 Udziweramiranji moyo wanga iwe?

Ndi kuzingwa m’kati mwanga?

Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamlemekeza tsopanonso,

Ndiye cipulumutso ca nkhope yanga ndi Mulungu wanga,