Masalmo 4

Pemphero posautsidwa

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Nesmoto. Salmo la Davide.

1 Pakupfuula ine mundiyankhe, Mulungu wa cilungamo canga;

Pondicepera mwandikulitsira malo:

Ndicitireni cifundo, imvani pemphero langa.

2 Amuna inu, ulemu wanga udzakhala wamanyazi kufikira liti?

Mudzakonda zacabe, ndi kufunafuna bodza kufikira liti?

3 Koma dziwani kuti Yehova anadzipatulira yekha womkondayo

Adzamva Yehova m’mene ndimpfuulira Iye,

4 Citani cinthenthe, ndipo musacimwe:

Nenani mumtima mwanu pakama panu, ndipo mukhale cete.

5 Iphani nsembe za cilungamo,

Ndipo mumkhulupirire Yehova.

6 Ambiri amati, Adzationetsa cabwino ndani?

Weramutsirani ife kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

7 Mwapatsa cimwemwe mumtima mwanga,

Cakuposa cao m’nyengo yakucuruka dzinthu zao ndi vinyo wao.

8 Ndi mtendere ndidzagona pansi, pomwepo ndidzagona tulo;

Cifukwa Inu, Yehova, mundikhalitsa ine, ndikhale bwino.