Masalmo 32

Mwai wa munthu amene Mulungu wamkhululukira

Cilangizo ca Davide.

1 Wodala munthuyo wokhululukidwa chimo lace;

Wokwiriridwa coipa cace.

2 Wodala munthuyu Yehova samwerengera mphulupulu zace;

Ndimo mumzimu mwace mulibe cinyengo.

3 Pamene ndinakhala cete mafupa anga anakalamba

Ndi kubuula kwanga tsiku lonse.

4 Cifukwa usana ndi usiku dzanja lanu linandilemera ine;

Uwisi wanga unasandulika kuuma kwa malimwe.

5 Ndinabvomera coipa canga kwa Inu;

Ndipo mphulupulu yanga sindinaibisa.

Ndinati, Ndidzaululira Yehova macimo anga;

Ndipo munakhululukira coipa ca kulakwa kwanga.

6 Cifukwa cace oyera mtima onse apemphere kwa Inu,

Pa nthawi ya kupeza Inu:

Indetu pakusefuka madzi akuru

Sadzamfikira iye.

7 Inu ndinu mobisalira mwanga; M’nsautso mudzandisunga;

Mudzandizinga ndi Nyimbo za cipulumutso.

8 Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo;

Ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang’ana iwe.

9 Musakhale monga kavalo, kapena ngati buru, wopanda nzeru:

Zomangira zao ndizo cam’kamwa ndi capamutu zakuwakokera,

Pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.

10 Zisoni zambiri zigwera woipa:

Koma cifundo cidzamzinga iye wakukhulupirira Yehova.

11 Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima;

Ndipo pfuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.