Masalmo 30

Mkwiyo wa Mulungu ukhala kanthawi, kuyanja kwao ndi kosatha

Salmo la Davide. Nyimbo yakuperekera nyumba kwa Mulungu.

1 Ndidzakukwezani, Yehova; pakuti mwandinyamutsa,

Ndipo simunandikondwetsera adani anga,

2 Yehova, Mulungu wanga,

Ndinapfuulira kwa Inu, ndipo munandiciritsa.

3 Yehova munabweza moyo wanga kumanda:

Munandisunga ndi moyo, kuti ndingatsikire kudzenje.

4 Yimbirani Yehova, inu okondedwa ace,

Ndipo yamikani pokumbukila ciyero cace.

5 Pakuti mkwiyo wace ukhala kanthawi kokha;

Koma kuyanja kwace moyo wonse:

Kulira kucezera,

Koma mamawa kuli kupfuula kukondwera.

6 Ndipo ine, ndinanena m’phindu langa,

Sindidzagwedezeka nthawi zonse.

7 Inu, Yehova, munakhazikitsa phiri langa ndi kuyanja kwanu:

Munabisa nkhope yanu; ndinaopa.

8 Ndinapfuulira kwa Inu, Yehova;

Kwa Yehova ndinapemba:

9 M’mwazi mwanga muli phindu lanji, potsikira ine kudzenje?

Ngati pfumbi lidzayamika Inu? ngati lidzalalikira coonadi canu?

10 Mverani, Yehova, ndipo ndicitireni cifundo:

Yehova, mundithandize ndi Inu.

11 Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera;

Munandibvula ciguduli canga, ndipo munandibveka cikondwero:

12 Kuti ulemu wanga uyimbire Inu, wosakhala cete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.