Masalmo 29

Acenjeza akuru alemekeze Mulungu

Salmo la Davide.

1 Perekani kwa Yehova, inu ana a amphamvu,

Perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

2 Perekani kwa Yehova ulemerero wa dzina lace:

Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa.

3 Liu la Yehova liri pamadzi;

Mulungu wa ulemerero agunda,

Ndiye Yehova pa madzi ambiri.

4 Liu la Yehova ndi lamphamvu;

Liu la Yehova ndi lalikurukuru.

5 Liu la Yehova lithyola mitengo yamkungudza;

Inde Yehova athyola mikungudza ya ku Lebano.

6 Aitumphitsa monga mwana wa ng’ombe;

Lebano ndi Sirio monga msona wa njati.

7 Liu la Yehova ligawa malawi a moto.

8 Liu la Yehova ligwedeza cipululu;

Yehova agwedeza cipululu ca Kadese.

9 Liu la Yehova liswetsa nyama zazikazi,

Ndipo lipulula nkhalango:

Ndipo m’Kacisi mwace zonse ziri m’mwemo zimati, Ulemerero:

10 Yehova anakhala pa Cigumula:

Inde Yehova akhala mfumu ku nthawi yomka muyaya.

11 Yehova adzapatsa anthu ace mphamvu:

Yehova adzadalitsa anthu ace ndi mtendere.