Masalmo 26

Davide popempha Mulungu amweruze, achula zokoma zace

Salmo la Davide.

1 Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda m’ungwiro wanga:

Ndipo ndakhulupirira Yehova, sindidzaterereka.

2 Mundiyesere, Yehova, ndipo mundisunthe;

Yeretsani imso zanga ndi mtima wanga.

3 Pakuti cifundo canu ciri pamaso panga;

Ndipo ndayenda m’coona canu.

4 Sindinakhala pansi ndi anthu acabe;

Kapena kutsagana nao anthu otyasika.

5 Ndidana nao msonkhano wa ocimwa,

Ndipo sindidzakhala nao pansi ocita zoipa.

6 Ndidzasamba manja anga mosalakwa;

Kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova:

7 Kuti ndimveketse mau a ciyamiko,

Ndi kulalikira nchito zanu zonse zozizwa.

8 Yehova, ndikonda cikhalidwe ca nyumba yanu,

Ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

9 Musandicotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa,

Kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi:

10 Amene m’manja mwao muli mphulupulu,

Ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.

11 Koma ine, ndidzayenda m’ungwiro wanga;

Mundiombole, ndipo ndicitireni cifundo.

12 Phazi langa liponda pacidikha:

M’masonkhano ndidzalemekeza Yehova.