Masalmo 24

Ulemerero wa Yehova

Salmo la Davide,

1 Dziko lapansi nla Yehova ndi zodzala zace zomwe,

Dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhala m’mwemo.

2 Pakuti Iye analimanga pazinyanja,

Nalikhazika pamadzi.

3 Adzakwera ndani m’phiri la Yehova?

Nadzaima m’malo ace oyera ndani?

4 Woyera m’manja, ndi woona m’mtima, ndiye;

Iye amene sanakweza moyo wace kutsata zacabe,

Ndipo salumbira monyenga,

5 Iye adzalandira dalitso kwa Yehova,

Ndi cilungamo kwa Mulungu wa cipulumutso cace.

6 Uwu ndi mbadwo wa iwo akufuna Iye,

Iwo akufuna nkhope yanu, Mulungu wa Yakobo.

7 Weramutsani mitu yanu, zipata inu;

Ndipo kwezekani inu, zitseko zosatha:

Kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.

8 Mfumu imene ya ulemerero ndani?

Yehova wamphamvu ndi wolimba,

Yehova wolimba kunkhondo.

9 Weramutsani mitu yanu, zipata inu;

Inde weramutsani, zitseko zosatha inu,

Kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.

10 Mfumu imene ya ulemerero ndani?

Yehova wa makamu makamu, Ndiye Mfumu ya ulemerero.