Masalmo 23

Amwai amene Yehova akhala Mbusa wao

Salimo la Davide,

1 Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

2 Andigonetsa ku busa lamsipu:

Anditsogolera ku madzi ndikha.

3 Atsitsimutsa moyo wanga;

Anditsogolera m’mabande a cilungamo, cifukwa ca dzina lace.

4 Inde, ndingakhale ndiyenda m’cigwa ca mthunzi wa Imfa,

Sindidzaopa coipa; pakuti Inu muli ndi ine:

Cibonga canu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine,

5 Mundiyalikira gome pamaso panga m’kuona kwa adani anga:

Mwandidzoza mutu wanga mafuta; cikho canga cisefuka.

6 Inde ukoma ndi cifundo zidzanditsata masiku onse a moyo wanga:

Ndipo ndidzakhala m’nyumba ya Yehova masiku onse.