Masalmo 22

Posautsidwa Davide adandaulira, apemphera, ayamika Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Ajelet Hasakara, Salmo la Davide.

1 Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?

Mukhaliranji kutali kwa cipulumutso canga, ndi kwa mau a kubuula kwanga?

2 Mulungu wanga, ndiitana usana, koma simubvomereza;

Ndipo usiku, sindikhala cete.

3 Koma Inu ndinu woyera,

Wakukhala m’malemekezo a Israyeli.

4 Makolo athu anakhulupirira Inu:

Anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.

5 Anapfuula kwa Inu, napulumutsidwa:

Anakhulupita Inu, ndipo sanacita manyazi.

6 Koma ine ndine nyongolotsi, si munthu ai:

Cotonza ca anthu, ndi wonyozedwa ndi anthu.

7 Onse akundipenya andiseka:

Akwenzula, apukusa mutu, nati,

8 Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa,

Amlanditse tsopano popeza akondwera naye.

9 Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa:

Wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.

10 Cibadwire ine anandisiyira Inu:

Kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.

11 Musandikhalire kutali; pakuti nsautso iri pafupi:

Pakuti palibe mthandizi.

12 Ng’ombe zamphongo zambiri zandizinga:

Mphongo zolimba za ku Basana zandizungulira,

13 Andiyasamira m’kamwa mwao,

Ngati mkango wozomola ndi wobangula.

14 Ndathiridwa pansi monga madzi,

Ndipo mafupa anga onse anaguluka:

Mtima wanga ukunga sera; Wasungunuka m’kati mwa matumbo anga,

15 Mphamvu yanga yauma ngati phale;

Ndi lilime langa likangamira ku nsaya zanga;

Ndipo mwandifikitsa ku pfumbi la imfa.

16 Pakuti andizinga agaru:

Msonkhano wa oipa wanditsekereza;

Andiboola m’manja anga ndi m’mapazi anga.

17 Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse;

Iwo ayang’ana nandipenyetsetsa ine:

18 Agawana zobvala zanga,

Nalota maere pa malaya anga,

19 Koma Inu, Yehova, musakhale kutari;

Mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.

20 Landitsani moyo wanga kulupanga;

Wokondedwa wanga ku mphamvu ya garu,

21 Ndipulumutseni m’kamwa mwa mkango;

Inde mwandiyankha ine ndiri pa nyanga za njati,

22 Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga:

Pakati pa msonkhano ndidzakulemekezani.

23 Inu akuopa Yehova, mumlemekeze;

Inu nonse mbumba ya Yakobo, mumcitire ulemu;

Ndipo mucite mantha ndi Iye, inu nonse mbumba ya Israyeli.

24 Pakuti sanapeputsa ndipo sananyansidwa ndi zunzo la wozunzika;

Ndipo sanambisira nkhope yace;

Koma pompfuulira Iye, anamva.

25 Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukuru:

Zowinda zanga ndidzazicita pamaso pa iwo akumuopa Iye.

26 Ozunzika adzadya nadzakhuta:

Adzayamika Yehova iwo amene amfuna:

Ukhale moyo mtima wako nthawi zonse.

27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukila nadzatembenukira kwa Yehova:

Ndipo mafuko onse a amitundu adzagwadira pamaso panu.

28 Pakuti ufumuwo ngwa Yehova;

Iye acita ufumu mwa amitundu.

29 Onenepa onse a pa dziko lapansi adzadya nadzagwadira:

Onse akutsikira kupfumbi adzawerama pamaso pace,

Ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wace.

30 Mbumba ya anthu idzamtumikira;

Kudzanenedwa za Ambuye ku mibadwo yakudza.

31 Iwo adzadza nadzafotokozera cilungamo cace

Kwa anthu akadzabadwa, kuti Iye anacicita.