Masalmo 21

Davide ayamika Mulungu pa kugonjetsa adani

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide,

1 Yehova, adzasekera mfumu mu mphamvu yanu;

Adzakondwera kwakukuru m’cipulumutso canu!

2 Mwampatsa iye cikhumbo ca mtimawace,

Ndipo simunakana pempho la milomo yace.

3 Pakuti mumkumika iye ndi madalitso okoma:

Muika korona wa golidi woyengetsa pamutu pace.

4 Anakupemphani moyo, mwampatsa iye;

Mwamtalikitsira masiku ku nthawi za nthawi.

5 Ulemerero wace ngwaukuru mwa cipulumutso canu:

Mumcitira iye ulemu ndi ukulu.

6 Pakuti mumuikira madalitso ku nthawi zonse;

Mumkondweretsa ndi cimwemwe pankhope panu.

7 Pakuti mfumu akhulupirira Yehova,

Ndipo mwa cifundo ca Wam’mwambamwamba sadzagwedezeka iye,

8 Dzanja lanu lidzapeza adani anu onse:

Dzanja lanu lamanja lidzapeza iwo akuda Inu.

9 Mudzawaika ngati ng’anjo yamoto pa nyengo ya mkwiyo wanu.

Yehova adzawatha m’kukwiya kwace,

Ndipo moto udzawanyeketsa.

10 Mudzaziononga zobala zao kuzicotsa pa dziko lapansi,

Ndi mbeu zao mwa ana a anthu.

11 Pakuti anakupangirani coipa:

Anapangana ciwembu, osakhoza kucicita.

12 Pakuti mudzawabweza m’mbuyo,

Popiringidza m’nsinga zanu pankhope pao,

13 Kwezekani, Yehova, mu mphamvu yanu:

Potero tidzayimba ndi kulemekeza cilimbiko canu.