Masalmo 16

Munthu wokhulupira Mulungu akhazikika mtima, osaopa kutayika

Mlkitamu wa Davide.

1 Ndisungeni ine, Mulungu: pakuti ndakhulupirira Inu.

2 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga:

Ndiribe cabwino cina coposa Inu.

3 Za oyera mtima okhala pa dziko lapansi,

Iwo ndiwo omveka mbiri, mwa iwowo muli cikondwero canga conse.

4 Zidzacuruka zisoni zao za iwo otsata mulungu wina:

Sindidzathira nsembe zao zamwazi,

Ndipo sindidzachula maina ao pakamwa panga,

5 Yehova ndiye gawo la colowa canga ndi cikho canga:

Ndinu wondigwirira colandira canga,

6 Zingwe zandigwera mondikondweretsa;

Inde cosiyira cokoma ndiri naco.

7 Ndidzadalitsa Yehova, amene anandicitira uphungu:

Usikunso imso zanga zindilangiza.

8 Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse:

Popeza ali pa dzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.

9 Cifukwa cace wasekera mtima wanga, nukondwera ulemu wanga;

Mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.

10 Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda;

Simudzalola wokondedwa wanu abvunde.

11 Mudzandidziwitsa njira ya moyo:

Pankhope panu pali cimwemwe cokwanira;

M’dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.