Masalmo 15

Cikhalidwe ca munthu woona wa Mulungu

Salmo la Davide.

1 Yehova, ndani adzagonera m’cihema mwanu?

Adzagonera ndani m’phiri lanu lopatulika?

2 Iye wakuyendayo mokwanira, nacita cilungamo,

Nanena zoonadi mumtima mwace.

3 Amene sasinjirira ndi lilime lace,

Sacitira mnzace coipa,

Ndipo satola msece pa mnansi wace.

4 M’maso mwace munthu woonongeka anyozeka;

Koma awacitira ulemu akuopa Yehova.

Atalumbira kwa tsoka lace, sasintha ai.

5 Ndarama zace sakongoletsa mofuna phindu lalikuru,

Ndipo salandira cokometsera mlandu kutsutsa wosacimwa.

Munthu wakucita izi sadzagwedezeka ku nthawi zonse,