Okhulupirira onse alemekeze Mulungu wao
1 Haleluya,
Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano,
Ndi cilemekezo cace mu msonkhano wa okondedwa ace.
2 Akondwere Israyeli mwa Iye amene anamlenga;
Ana a Ziyoni asekere mwa Mfumu yao.
3 Alemekeze dzina lace ndi kuthira mang’ombe;
Amyimbire zomlemekeza ndi lingaka ndi zeze.
4 Popeza Yehova akondwera nao anthu ace;
Adzakometsa ofatsa ndi cipulumutso,
5 Okondedwa ace atumphe mokondwera m’ulemu:
Apfuule mokondwera pamakama pao,
6 Nyimbo zakukweza Mulungu zikhale pakamwa pao,
Ndi lupanga lakuthwa konse konse m’dzanja lao;
7 Kubwezera cilango akunja,
Ndi kulanga mitundu ya anthu;
8 Kumanga mafumu ao ndi maunyolo,
Ndi omveka ao ndi majerejede acitsulo;
9 Kuwacitira ciweruzo colembedwaco:
Ulemu wa okondedwa ace onse ndi uwu.
Haleluya.