Masalmo 148

Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu

1 Haleluya.

Lemekezani Yehova kocokera kumwamba;

Mlemekezeni m’misanje.

2 Mlemekezeni, angelo ace onse;

Mlemekezeni, makamu ace onse.

3 Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi;

Mlemekezeni, nyenyezi zonse zaunikira.

4 Mlemekezeni, m’mwambamwamba,

Ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.

5 Alemekeze dzina la Yehova;

Popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

6 Anazikhazikanso ku nthawi za nthawi;

Anazipatsa cilamulo cosatumphika.

7 Lemekezani Yehova kocokera ku dziko lapansi,

Zinsomba inu, ndi malo ozama onse;

8 Moto ndi matalala, cipale cofewa ndi nkhungu;

Mphepo ya namondwe, yakucita mau ace;

9 Mapiri ndi zitunda zonse;

Mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:

10 Nyama za kuthengo ndi zoweta zonse;

Zokwawa, ndi mbalame zakuuluka;

11 Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu;

Zinduna ndi oweruza onse a padziko;

12 Anyamata ndiponso anamwali;

Okalamba pamodzi ndi ana:

13 Alemekeze dzina la Yehova;

Pakuti dzina lace lokha ndi lokwezeka;

Ulemerero wace uli pamwamba pa dziko lapansi ndi thambo.

14 Ndipo anakweza nyanga ya anthu ace,

Cilemekezo ca okondedwa ace onse;

Ndiwo ana a Israyeli, anthu a pafupi pa Iye,

Haleluya,