Masalmo 14

Anthu oipadi

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salmo la Davide.

1 Waucitsiru amati mumtima mwace, Kulibe Mulungu.

Acita zobvunda, acita nchito zonyansa;

Kulibe wakucita bwino.

2 Yehova m’Mwamba anaweramira pa ana a anthu,

Kuti aone ngati aliko wanzeru,

Wakufuna Mulungu.

3 Anapatuka onse; pamodzi anabvunda mtima;

Palibe wakucita bwino ndi mmodzi yense.

4 Kodi onse ocita zopanda pace sadziwa kanthu?

Pakudya anthu anga monga akudya mkate,

Ndipo saitana pa Yehova.

5 Pamenepa anaopa-opatu:

Pakuti Mulungu ali mu mbadwo wa wolungama.

6 Munyazitsa uphungu wa wozunzika,

Koma Yehova ndiye pothawira pace.

7 Mwenzi cipulumutso ca Israyeli citacokera ku Ziyoni!

Pakubweretsa Yehova anthu ace a m’nsinga,

Pamenepo adzakondwera Yakobo, nadzasekera Israyeli.