Masalmo 136

Mulungu alemekezedwe pa cifundo cace

1 Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

2 Yamikani Mulungu wa milungu:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

3 Yamikani Mbuye wa ambuye:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

4 Amene yekha acita zodabwiza zazikuru:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

5 Amene analenga zakumwamba mwanzeru:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

6 Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

7 Amene analenga miuni yaikuru:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

8 Dzuwa liweruze usana:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

9 Mwezi ndi nyenyezi ziweruze usiku;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

10 Iye amene anapandira Aaigupto ana ao oyamba:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

11 Naturutsa Israyeli pakati pao;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

12 Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

13 Amene anagawa magawo Nyanja Yofiira:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

14 Napititsa Israyeli pakati pace;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

15 Nakhutula Farao ndi khamu lace m’Nyanja Yofiira:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

16 Amene anatsogolera anthu ace m’cipululu:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

17 Amene anapanda mafumu akulu:

Pakuti cifundo cace ncosatha,

18 Ndipo anawapha mafumu omveka:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

19 Sihoni mfumu ya Aamori;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

20 Ndi ogi mfumu ya Basana:

Pakuti cifundo cace ncosatha.

21 Ndipo anaperekadzikolaolikhale cosiyira;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

22 Cosiyira ca kwa Israyeli mtumiki wace;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

23 Amene anatikumbukila popepuka ife;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

24 Natikwatula kwa otisautsa;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

25 Ndiye wakupatsa nyama zonse cakudya;

Pakuti cifundo cace ncosatha.

26 Yamikani Mulungu wa kumwamba,

Pakuti cifundo cace ncosatha.