Masalmo 135

Mulungu alemekezedwa pa ukulu wace. Mafano ndi acabe

1 Haleluya;

Lemekezani dzina la Yehova;

Lemekezani inu atumiki a Yehova:

2 Inu akuimirira m’nyumba ya Yehova,

M’mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino;

Muyimbire zolemekeza dzina lace; pakuti nkokondweretsa kutero.

4 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo,

Israyeli, akhale cuma cace ceni ceni.

5 Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkuru,

Ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.

6 Ciri conse cimkonda Yehova acicita,

Kumwamba ndi pa dziko lapansi, m’nyanja ndi mozama monse.

7 Akweza mitambo icokere ku malekezero a dziko lapansi;

Ang’animitsa mphezi zidzetse mvula;

Aturutsa mphepo mosungira mwace.

8 Anapanda oyamba a Aigupto,

Kuyambira munthu kufikira zoweta.

9 Anatumiza zizindikilo ndi zodabwiza pakati pako,

Aigupto iwe, Pa Farao ndi pa omtumikira onse.

10 Ndiye amene anapanda amitundu ambiri.

Napha mafumu amphamvu;

11 Sihoni mfumu ya Aamori,

Ndi Ogi mfumu ya Basana,

Ndi maufumu onse a Kanani:

12 Ndipo anapereka dziko lao likhale cosiyira,

Cosiyira ca kwa Israyeli anthu ace.

13 Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;

Cikumbukilo canu, Yehova, kufikira mibadwo mibadwo.

14 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ace,

Koma adzaleka atumiki ace.

15 Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golidi,

Nchito ya manja a anthu.

16 Pakamwa ali napo koma osalankhula;

Maso ali nao, koma osapenya;

17 Makutu ali nao, koma osamva;

Inde, pakamwa pao palibe mpweya.

18 Akuwapanga adzafanana nao;

Inde, onse akuwakhulupirira.

19 A nyumba ya Israyeli inu, lemekezani Yehova:

A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:

20 A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova:

Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.

21 Alemekezedwe Yehova kucokera m’Ziyoni,

Amene akhala m’Yerusalemu.

Haleluya,